Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 5:4-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo ine ndinati, Ndithu amenewo ali aumphawi; ali opusa; pakuti sadziwa njira ya Yehova, kapena ciweruzo ca Mulungu wao.

5. Ine ndidzanka kwa akuru, ndidzanena ndi iwo; pakuti adziwa njira ya Yehova, ndi ciweruzo ca Mulungu wao. Koma awa anabvomerezana natyola gori, nadula zomangira zao.

6. Cifukwa cace mkango woturuka m'nkhalango udzawapha, ndi mmbulu wa madzulo udzawafunkha, nyalugwe adzakhalira m'midzi mwao, onse amene aturukamo adzamwetulidwa; pakuti zolakwa ziri zambiri, ndi mabwerero ao acuruka.

7. Bwanji ndidzakhululukira iwe? pamenepo ana ako andisiya Ine, nalumbira pa iyo yosati milungu; pamene ndinakhutitsa iwo, anacita cigololo, nasonkhana masonkhano m'nyumba za adama.

8. Anali onga akavalo okhuta mamawa; yense wakumemesera mkazi wa mnansi wace.

9. Kodi sindidzawalanga cifukwa ca zimenezi? ati Yehova; kodi moyo wanga sudzabwezera cilango mtundu woterewu?

10. Kwerani pa makoma ace nimupasule; koma musatsirize konse; cotsani nthambi zace pakuti siziri za Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 5