Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 5:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Phodo lao liri ngati manda apululu, onsewo ndiwo olimba.

17. Adzadya zokolola zako, ndi mkate wako, umene ana ako amuna ndi akazi ayenera kudya; adzadya nkhosa zako ndi zoweta zako; adzadya mphesa zako ndi nkhuyu zako; adzapasula ndi lupanga midzi yamalinga yako, imene ukhulupiriramo.

18. Koma masiku onsewo, ati Yehova, sindidzatsirizitsa konse ndi iwe.

19. Ndipo padzakhala: pamene mudzati, Cifukwa canji Yehova Mulungu wathu aticitira ife zonse izi? ndipo udzayankha kwa iwo, Monga ngati mwandisiya Ine, ndi kutumikira milungu yacilendo m'dziko lanu, momwemo mudzatumikira alendo m'dziko siliri lanu.

20. Nenani ici m'nyumba ya Yakobo, lalikirani m'Yuda, kuti,

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 5