32. Ndipo ngamila zao zidzakhala zofunkha, ndi unyinji wa ng'ombe zao udzakhala wolanda; ndipo ndidzabalalitsira ku mphepo zonse iwo amene ameta m'mbali mwa tsitsi lao; ndipo ndidzatenga tsoka lao ku mbali zao zonse, ati Yehova.
33. Ndipo Hazori adzakhala mokhalamo ankhandwe, bwinja lacikhalire; simudzakhalamo munthu, simudzagonamo mwana wa munthu.
34. Mau a Yehova amene anafika kwa Yeremiya mneneri, onena za Elamu poyamba kulamulira Zedekiya mfumu ya Yuda, kuti,
35. Yehova wa makamu atero: Taonani, ndidzatyola uta wa Elamu, ndiwo mtima wa mphamvu yao.