Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 41:8-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Koma mwa iwo anaoneka anthu khumi amene anati kwa Ismayeli, Musatiphe ife; pakuti tiri ndi cuma cobisika m'mudzi, ca tirigu, ndi ca barele, ndi ca mafuta, ndi ca uci. Momwemo analeka, osawapha pakati pa abale ao.

9. Ndipo dzenje moponyamo Ismayeli mitembo yonse ya anthu amene anawapha, cifukwa ca Gedaliya, ndilo analipanga mfumu Asa cifukwa ca kuopa Raasa mfumu ya Israyeli, lomwelo Ismayeli mwana wa Netaniya analidzaza ndi ophedwawo.

10. Ndipo Ismayeli anatenga ndende otsala onse a anthu okhala m'Mizipa, ana akazi a mfumu, ndi-anthu onse amene anatsala m'Mizipa, amene Nebuzaradani kapitao wa alonda anapatsira Gedaliya mwana wa Ahikamu; Ismayeli mwana wa Netaniya anawatenga ndende, napita kukaolokera kwa ana a Amoni.

11. Koma pamene Yohanani mwana wa Kareya, ndi akazembe Onse a nkhondo akhala naye, anamva zoipa zonse anazicita Ismayeli mwana wa Netaniya,

12. anatenga anthu onse, nanka kukamenyana ndi Ismayeli mwana wa Netaniya, nampeza pa madzi ambiri a m'Gibeoni.

13. Ndipo panali pamene anthu onse amene anali ndi Ismayeli anaona Yohanani mwana wa Kareya, ndi akazembe onse a nkhondo okhala naye, anasekera.

14. Ndipo anthu onse amene Ismayeli anatenga ndende kuwacotsa m'Mizipa anatembenuka nabwera, nanka kwa Yohanani mwana wace wa Kareya,

15. Koma Ismayeli mwana wace wa Netaniya anapulumuka Yohanani ndi anthu asanu ndi atatu, nanka kwa ana a Amoni.

16. Ndipo Yohanani mwana wace wa Kareya ndi akazembe onse a makamu amene anali naye, anatenga anthu onse otsala a ku Mizipa, amene anawabweza kwa Ismayeli mwana wace wa Netaniya atapha Gedaliya mwana wace wa Ahikamu, anthu a nkhondo, ndi akazi, ndi ana, ndi adindo, amene anawabwezanso ku Gibeoni;

17. ndipo anacoka, natsotsa m'Geruti-Kimamu, amene ali ku Betelehemu, kunka kulowa m'Aigupto,

18. cifukwa ca Akasidi; pakuti anawaopa, cifukwa Ismayeli mwana wace wa Netaniya anapha Gedaliya mwana wace wa Akikamu, amene mfumu ya ku Babulo anamuika wolamulira m'dzikomo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 41