Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 38:8-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ebedi-Meleki anaturuka m'nyumba ya mfumu, nanena ndi mfumu, kuti,

9. Mbuyanga mfumu, anthu awa anacita zoipa m'zonse anacitira Yeremiya mneneri, amene anamponya m'dzenje; ndipo afuna kufa m'menemo cifukwa ca njala; pakuti mulibe cakudya cina m'mudzimu.

10. Ndipo mfumu inamuuza Ebedi-Meleki Mkusi, kuti, Tenga anthu makumi atatu, umkweze numturutse Yeremiya mneneri m'dzenjemo, asanafe.

11. Ndipo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, nalowa nao m'nyumba ya mfumu ya pansi pa nyumba ya cuma, natenga m'menemo nsaru zakale zotaya ndi zansanza zobvunda, nazitsitsira ndi zingwe kwa Yeremiya m'dzenjemo.

12. Ndipo Ebedi-Meleki Mkusi anati kwa Yeremiya, Kulungatu zingwe ndi nsaruzi zotaya zakale ndi zansanza ndi kuzikwapatira. Ndipo Yeremiya anacita comweco.

13. Ndipo anamkweza Yeremiya ndi zingwe, namturutsa m'dzenjemo; ndipo Yeremiya anakhalabe m'bwalo la kaidi.

14. Ndipo mfumu Zedekiya anatuma, natntenga Yeremiya mneneri nalowa naye m'khomo lacitatu la nyumba ya Yehova; ndipo mfumu inati kwa Yeremiya, Ndidzakufunsa iwe kanthu; usandibisire ine kanthu.

15. Ndipo Yeremiya anati kwa Zedekiya, Ndikakufotokozerani, kodi simudzandipha ine? ndipo ndikakupangirani, simudzandimveta ine.

16. Ndipo Zedekiya analumbira m'tseri kwa Yeremiya, kuti, Pali Yehova, amene anatilengera ife moyo uno, sindidzakupha iwe sindidzakupereka iwe m'manja mwa anthu awa amene afuna moyo wako.

17. Ndipo Yeremiya anati kwa Zedekiya, Atero Yehova, Mulungu wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Ngati mudzaturukira kwa akuru a mfumu ya ku Babulo, mudzakhala ndi moyo, ndipo mudziwu sudzatenthedwa ndi moto; ndipo mudzakhala ndi moyo ndi banja lanu;

18. koma ngati simudzaturukira kwa akuru a mfumu ya ku Babulo, mudziwu udzaperekedwa m'dzanja la Akasidi, ndipo udzatenthedwa ndi moto, ndipo simudzapulumuka m'manja mwao.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 38