Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 38:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo Ebedi-Meleki Mkusi anati kwa Yeremiya, Kulungatu zingwe ndi nsaruzi zotaya zakale ndi zansanza ndi kuzikwapatira. Ndipo Yeremiya anacita comweco.

13. Ndipo anamkweza Yeremiya ndi zingwe, namturutsa m'dzenjemo; ndipo Yeremiya anakhalabe m'bwalo la kaidi.

14. Ndipo mfumu Zedekiya anatuma, natntenga Yeremiya mneneri nalowa naye m'khomo lacitatu la nyumba ya Yehova; ndipo mfumu inati kwa Yeremiya, Ndidzakufunsa iwe kanthu; usandibisire ine kanthu.

15. Ndipo Yeremiya anati kwa Zedekiya, Ndikakufotokozerani, kodi simudzandipha ine? ndipo ndikakupangirani, simudzandimveta ine.

16. Ndipo Zedekiya analumbira m'tseri kwa Yeremiya, kuti, Pali Yehova, amene anatilengera ife moyo uno, sindidzakupha iwe sindidzakupereka iwe m'manja mwa anthu awa amene afuna moyo wako.

17. Ndipo Yeremiya anati kwa Zedekiya, Atero Yehova, Mulungu wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Ngati mudzaturukira kwa akuru a mfumu ya ku Babulo, mudzakhala ndi moyo, ndipo mudziwu sudzatenthedwa ndi moto; ndipo mudzakhala ndi moyo ndi banja lanu;

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 38