Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 36:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo Baruki anawerenga m'buku mau a Yeremiya m'nyumba ya Yehova, m'cipinda ca Gemariya mwana wa Safani mlembi, m'bwalo la kumtunda, pa khomo la cipata catsopano ca nyumba ya Yehova, m'makutu a anthu onse.

11. Pamene Mikaya mwana wa Hemariya, mwana wa Safani, anamva m'buku mau onse a Yehova,

12. anatsikira ku nyumba ya mfumu, nalowa m'cipinda ca mlembi; ndipo, taonani, akuru onse analikukhalamo, Elisama mlembi, ndi Delaya mwana wa Semaya, ndi Elinatani mwana wa Akibori, ndi Gemariya mwana wa Safani, ndi Zedekiya mwana wa Hananiya, ndi akuru onse.

13. Ndipo Makaya anafotokozera iwo mau onse amene anamva, pamene Baruki anawerenga buku m'makutu a anthu.

14. Cifukwa cace akuru onse anatuma Yehudi mwana wa Nataniya, mwana wa Salamiya, mwana wa Kusa, kwa Baruki, kukanena, Tenga m'dzanja lako mpukutu wauwerenga m'makutu a anthu, nudze kuno. Ndipo Baruki mwana wa Neriya anatenga mpukutuwo m'dzanja lace, nadza kwa iwo.

15. Ndipo anati kwa iye, Khala pansi tsopano, nuwerenge m'makutu athu. Ndipo Baruki anauwerenga m'makutu ao.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 36