Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 34:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo ndidzapereka anthu akulakwira pangano langa, amene sanacita mau a pangano limene anapangana pamaso panga, muja anadula pakati mwana wa ng'ombe ndi kupita pakati pa mbali zace;

19. akulu a Yuda, ndi akulu a Yerusalemu, adindo, ndi ansembe, ndi anthu onse a m'dziko, amene anapita pakati pa mbali za mwana wa ng'ombe;

20. ndidzapereka iwo m'dzanja la adani ao, ndi m'dzanja la iwo akufuna moyo wao; ndipo mitembo yao idzakhala cakudya ca mbalame za mlengalenga, ndi ca zirombo za pa dziko lapansi.

21. Ndipo Zedekiya mfumu ya Yuda ndi akulu ace ndidzawapereka m'dzanja la adani ao, ndi m'dzanja la akufuna moyo wao, ndi m'dzanja la nkhondo ya mfumu ya ku Babulo, imene yakucokerani.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 34