Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 34:16-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. koma mwabwerera ndi kuipitsa dzina langa, ndi kubwezera m'ukapolo yense kapolo wace wamwamuna, ndi wamkazi, amene munammasula akacite zao, ndipo munawagonjetsa, akhale akapolo anu amuna ndi akazi.

17. Cifukwa cace Yehova atero: Simunandimvera Ine, kuti mulalikire ufulu, munthu yense kwa mbale wace, ndi munthu yense kwa mnzace; taonani, ndilalikira kwa inu ufulu, ati Yehova, wa kulupanga, kucaola, ndi kunjala; ndipo ndidzakuperekani mukhale oopsetsa m'maufumu onse a dziko lapansi.

18. Ndipo ndidzapereka anthu akulakwira pangano langa, amene sanacita mau a pangano limene anapangana pamaso panga, muja anadula pakati mwana wa ng'ombe ndi kupita pakati pa mbali zace;

19. akulu a Yuda, ndi akulu a Yerusalemu, adindo, ndi ansembe, ndi anthu onse a m'dziko, amene anapita pakati pa mbali za mwana wa ng'ombe;

20. ndidzapereka iwo m'dzanja la adani ao, ndi m'dzanja la iwo akufuna moyo wao; ndipo mitembo yao idzakhala cakudya ca mbalame za mlengalenga, ndi ca zirombo za pa dziko lapansi.

21. Ndipo Zedekiya mfumu ya Yuda ndi akulu ace ndidzawapereka m'dzanja la adani ao, ndi m'dzanja la akufuna moyo wao, ndi m'dzanja la nkhondo ya mfumu ya ku Babulo, imene yakucokerani.

22. Taonani, ndidzauza, ati Yehova, ndidzabwezera iwo ku mudzi uno; ndipo adzamenyana nao, nadzaulanda, nadzautentha ndi moto; ndipo ndidzayesa midzi ya Yuda mabwinja, palibenso wokhalamo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 34