Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 34:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mau amene anadza kwa Yeremiya kucokera kwa Yehova, pamene Nebukadinezara mfumu ya Babulo, ndi nkhondo yace yonse, ndi maufumu onse a dziko lapansi amene anagwira mwendo wace, ndi anthu onse, anamenyana ndi Yerusalemu, ndi midzi yace yonse, akuti:

2. Yehova Mulungu wa Israyeli atero, Pita, nena kwa Zedekiya mfumu ya Yuda, numuuze iye, kuti Yehova atero, Taona, ndidzapereka mudziwu m'dzanja la mfumu ya ku Babulo, ndipo adzautentha ndi moto;

3. ndipo iwe sudzapulumuka m'dzanja lace, koma udzagwiridwadi, nudzaperekedwa m'dzanja lace; ndipo maso ako adzaanana nao a mfumu ya ku Babulo, ndipo iye adzanena nawe pakamwa ndi pakamwa, ndipo udzanka ku Babulo.

4. Koma tamva mau a Yehova, iwe Zedekiya mfumu ya Yuda; Yehova atero za iwe, Sudzafa ndi lupanga;

5. udzafa ndi mtendere; ndipo adzawambika iwe monga anawambika makolo ako, mafumu akale usanakhale iwe; ndipo adzakulirira iwe, kuti, Kalanga ine ambuye! pakuti ndanena mau, ati Yehova.

6. Ndipo Yeremiya mneneri ananena mau onsewa kwa Zedekiya mfumu ya Yuda m'Yerusalemu,

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 34