Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 31:35-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. Yehova atero, amene apatsa dzuwa kuti liunikire usana, ndi malemba a mwezi ndi a nyenyezi kuti aunikire usiku, amene atonthoza nyanja, pamene mafunde ace agabvira; Yehova wa makamu ndi dzina lace:

36. Ngati malembawa acoka pamaso panga, ati Yehova, pamenepo mbeunso ya Israyeli idzaleka kukhala mtundu pamaso panga ku nthawi zonse.

37. Atero Yehova, Ngati ukhoza kuyesa thambo la kumwamba, ndi kusanthula pansi maziko a dziko, pamenepo ndidzacotsa mbeu zonse za Israyeli cifukwa ca zonse anazicita, ati Yehova.

38. Taonani, masiku adza, ati Yehova, amene mudziwu udzamangidwira Yehova kuyambira pa nsanja ya Hananeli kufikira ku cipata ca kungondya.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 31