Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 30:3-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pakuti, taona, masiku adzadza, ati Yehova, amene ndidzabwezanso undende wa anthu anga Aisrayeli ndi Ayuda, ati Yehova; ndipo ndidzawabwezera ku dziko limene ndinapatsa makolo ao. Ndipo adzakhala nalo.

4. Awa ndi mau ananena Yehova za Israyeli ndi Yuda.

5. Pakuti Yehova atero: Tamva ife mau akunthunthumira, ndi amantha, si amtendere.

6. Funsani tsopano, ndi kuona ngati mwamuna aona mwana; cifukwa canji ndiona mwamuna ndi manja ace pa cuuno cace, monga mkazi alinkubala, ndi nkhope zao zotumbuluka?

7. Kalanga ine! pakuti nlalikuru tsikulo, palibe lina lotere; ndi nthawi ya msauko wa Yakobo; koma adzapulumuka m'menemo.

8. Pakuti padzakhala tsiku lomwelo, ati Yehova wa makamu, kuti ndidzatyola gori lace pakhosi pako, ndipo ndidzadula zomangira zako; ndipo alendo sadzamuyesanso iye mtumiki wao;

9. koma adzamtumikira Yehova Mulungu wao, ndi Davide mfumu yao, imene ndidzawaukitsira.

10. Ndipo usaope, iwe Yakobo mtumiki wanga, ati Yehova; usaope, iwe Israyeli; pakuti, taona, ndidzakupulumutsa iwe kutari, ndi mbeu zako ku dziko la undende wao; ndipo Yakobo adzabwera, nadzakhala ndi mtendere, ndipo adzakhala cete, palibe amene adzamuopsya.

11. Pakuti Ine ndiri ndi iwe, ati Yehova, kuti ndipulumutse iwe; koma ndidzatha ndithu amitundu onse amene ndinakumwazira mwa iwo, koma sindidzatha iwe ndithu; koma ndidzakulangiza iwe ndi ciweruziro, ndipo sindidzakuyesa wosaparamula.

12. Pakuti atero Yehova, Kulaswa kwako kuti kosapoleka ndi bala lako liri lowawa.

13. Palibe amene adzanenera mlandu wako, ulibe mankhwala akumanga nao bala lako.

14. Mabwenzi ako onse anakuiwala iwe; salikukufuna iwe; pakuti ndakulasa ndi bala la mdani, ndi kulanga kwa wankhanza; cifukwa ca mphulupulu yako yaikuru, cifukwa zocimwa zako zinacuruka.

15. Cifukwa canji ulilira bala lako? kuphwetekwa kwako kuli kosapoleka; cifukwa ca mphulupulu yako yaikuru, cifukwa zocimwa zako zinacuruka, ndakucitira iwe izi.

16. Cifukwa cace iwo akulusira iwe adzalusidwanso; ndi adani ako onse, adzanka kuundende onsewo; ndipo iwo adzakufunkha iwe adzakhala cofunkha, ndipo onse akulanda iwe ndidzapereka kuti zilandidwe zao.

17. Pakuti ndidzakubwezera iwe moyo, ndipo ndidzapoletsa mabala ako, ati Yehova; cifukwa anacha iwe wopitikitsidwa, nati, Ndiye Ziyoni, amene kulibe munthu amfuna.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 30