Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 3:9-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo kunali kuti mbiri ya dama lace inaipitsa dziko, ndipo anacita cigololo ndi miyala ndi mitengo.

10. Ndipo zingakhale zonsezi mphwace wonyenga sanabwera kwa Ine ndi mtima wace wonse, koma monama, ati Yehova.

11. Ndipo Yehova anati kwa ine, Israyeli wobwerera anadzionetsa wolungama kopambana ndi Yuda wonyenga,

12. Pita; nulalikire mau awa kuyang'ana kumpoto, ndi kuti, Bwera iwe Israyeli wobwerera, ati Yehova; sindidzakuyang'anira iwe ndi kukwiya; pakuti Ine ndiri wacifundo, ati Yehova, sindidzakhala nako kukwiya ku nthawi zonse.

13. Koma bvomereza zoipa zako, kuti walakwira Yehova Mulungu wako, ndi kupatukira mwa alendo patsinde pa mitengo yaiwisi yonse, ndipo sunamvera mau anga, ati Yehova.

14. Bwerani, ananu obwerera, ati Yehova; pakuti Ine ndine mbuye wanu; ndipo ndidzakutengani inu mmodzi mmodzi wa pa mudzi uli wonse, ndi awiri awiri a pa banja liri lonse, ndi kukutengerani ku Ziyoni;

15. ndipo ndidzakupatsani inu abusa monga mwa mtima wanga, adzakudyetsani inu nzeru ndi luntha.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 3