Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 29:23-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. cifukwa anacita zopusa m'Israyeli, nacita cigololo ndi akazi a anansi ao, nanena mau onama m'dzina langa, amene ndinawauza kuti asanene; Ine ndine wodziwa, ndi mboni, ati Yehova.

24. Ndipo za Semaya Mnehelamu uzinena, kuti,

25. Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli, kuti, Cifukwa watumiza akalata m'dzina lako iwe mwini kwa anthu onse amene akhala ku Yerusalemu, ndi kwa Zefaniya mwana wace wa Maseya wansembe, ndi kwa ansembe onse, kuti.

26. Yehova anakuyesa iwe wansembe m'malo mwa Yehoyada wansembe, kuti iwe ndi anzako mudzakhale akapitao m'nyumba ya Yehova, oyang'anira munthu yense wamisala, wodziyesa mneneri, kuti umuike iye m'zigologolo ndi m'gori.

27. Ndipo tsopano, walekeranji kumdzudzula Yeremiya wa ku Anatoti, amene amadziyesa mneneri wanu,

28. popeza watitumizira mau ku Babulo, akuti, Undende udzakhalitsa; mangani nyumba, khalani m'menemo; limani minda, idyani zipatso zao?

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 29