13. Mudzaferanji, iwe ndi anthu anu, ndi lupanga ndi njala, ndi caola, monga wanena Yehova za mtundu umene ukana kumtumikira mfumu ya ku Babulo?
14. Musamvere mau a aneneri amene anena ndi inu, kuti, simudzamtumikira mfumu ya ku Babulo; pakuti akunenerani zonama.
15. Pakuti sindinawatuma iwo, ati Yehova, koma anenera zonama m'dzina langa; kuti ndikupitikitseni inu, kuti mudzathedwe, inu, ndi aneneri amene anenera kwa inu.
16. Ndiponso ndinanena kwa ansembe ndi kwa anthu onsewa, kuti, Yehova atero: Musamvere mau a aneneri anu amene akunenerani inu, kuti, Taonani, zipangizo za nyumba ya Yehova zidzatengedwanso ku Babulo posacedwa; pakuti akunenerani inu zonama.
17. Musamvere amenewa; mtumikireni mfumu ya ku Babulo, ndipo mudzakhala ndi moyo; cifukwa canji mudzi uwu udzakhala bwinja?