Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 27:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Koma mtundu umene udzaika khosi lao pansi pa gori la mfumu ya ku Babulo, ndi kumtumikira iye, mtundu umene ndidzaulola ukhalebe m'dziko lao, ati Yehova; ndipo adzalilima, nadzakhala momwemo.

12. Ndipo ndinanena kwa Zedekiya mfumu ya Yuda monga mau onse amenewa, kuti, Longani makosi anu m'gori la mfumu ya ku Babulo, ndi kumtumikira iye ndi anthu ace, ndipo mudzakhala ndi moyo.

13. Mudzaferanji, iwe ndi anthu anu, ndi lupanga ndi njala, ndi caola, monga wanena Yehova za mtundu umene ukana kumtumikira mfumu ya ku Babulo?

14. Musamvere mau a aneneri amene anena ndi inu, kuti, simudzamtumikira mfumu ya ku Babulo; pakuti akunenerani zonama.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 27