Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 25:18-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Yerusalemu, ndi midzi ya Yuda, ndi mafumu ace omwe, ndi akuru ace, kuwayesa iwo bwinja, cizizwitso, cotsonyetsa, ndi citemberero; monga lero lino;

19. Farao mfumu ya ku Aigupto, ndi atumiki ace, ndi akuru ace, ndi anthu ace onse;

20. ndi anthu onse osanganizidwa, ndi mafumu onse a dziko la Uzi, ndi mafumu onse a dziko la Afilisti, ndi Asikeloni, ndi Gaza, ndi Ekroni, ndi otsala a Asdodi,

21. Edomu, ndi Moabu, ndi ana a Amoni,

22. ndi mafumu onse a Turo, ndi mafumu onse a Zidoni, ndi mafumu a cisumbu cimene ciri patsidya pa nyanja;

23. Dedani, ndi Tema, ndi Buzi, ndi onse amene ameta m'mbali mwa tsitsi;

24. ndi mafumu onse a Arabiya, ndi mafumu onse a anthu osanganizidwa okhala m'cipululu;

25. ndi mafumu onse a Zimiri, ndi mafumu onse a Elamu, ndi mafumu onse a Medi,

26. ndi mafumu onse a kumpoto, a kutari ndi a kufupi, wina ndi mnzace; ndi maufumu onse a dziko lapansi, okhala pansi pano; ndi mfumu ya Sesaki adzamwa pambuyo pao.

27. Ndipo uziti kwa iwo, Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Imwani inu, ndi kuledzera, ndi kusanza, ndi kugwa, osanyamukanso konse, cifukwa ca lupanga limene ndidzatumiza mwa inu.

28. Ndipo padzakhala, ngati akana kutenga cikho pa dzanja lako kuti amwe, uziti kwa iwo, Yehova wa makamu atero: Kumwa muzimwa.

29. Pakuti, taonani, ndiyamba kucita coipa pa mudzi umene uchedwa ndi dzina langa, kodi inu mudzakhala osalangidwa konse? Simudzakhala osalangidwa; pakuti ndidzaitana lupanga ligwe pa onse okhala m'dziko lapansi, ati Yehova wa makamu.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 25