Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 16:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndiponso mau a Mulungu anadza kwa ine, kuti,

2. Usatenge mkazi, usakhale ndi ana amuna ndi akazi m'malo muno.

3. Pakuti Yehova atero za ana amuna ndi za ana akazi akubadwa m'malo muno, ndi za amai anawabala iwo, ndi za atate ao anawabala iwo m'dziko muno:

4. Adzafa ndi imfa zanthenda; sadzaliridwa maliro, sadzaikidwa; adzakhala ngati ndowe panthaka; ndipo adzathedwa lupanga, ndi njala; ndipo mitembo yao idzakhala cakudya ca mbalame za kumlengalenga, ndi zirombo za dziko lapansi.

5. Pakuti Yehova atero, Usalowe m'nyumba ya maliro, usanke kukacita maliro ao, kapena kuwalirira; pakuti ndacotsa mtendere wanga pa anthu awa, cifundo ndi nsoni zokoma, ati Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 16