Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 13:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo ndinapita, ndinaubisa pa Firate, monga Yehova anandiuza ine.

6. Ndipo panali atapita masiku ambiri, kuti Yehova anati kwa ine, Uka, pita ku Firate, nukatenge kumeneko mpango uja, ndinakuuza iwe ukaubise kumeneko.

7. Ndipo ndinanka ku Firate, ndikumba, nditenga mpango m'malo m'mene ndinaubisamo; ndipo, taonani, mpango unaonongeka, wosayenera kanthu.

8. Ndipo mau a Yehova anadza kwa ine, kuti,

9. Yehova atero, Momwemo ndidzaononga kudzitama kwa Yuda, ndi kudzitama kwakukuru kwa Yerusalemu.

10. Anthu oipa awa, amene akana kumva mau anga, amene ayenda m'kuumirira kwa mtima wao, atsata milungu yina kuitumikira, ndi kuigwadira, adzakhala ngati mpango uwu, wosayenera kanthu.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 13