19. Ndipo akumwela adzakhala nalo phiri la Esau colowa cao; ndi iwo a kucidikha adzakhala nalo dziko la Afilisti; ndipo adzakhala nayo minda ya Efraimu, ndi minda ya Samariya colowa cao; ndi Benjamini adzakhala nalo la Gileadi.
20. Ndipo andende a khamu ili la ana a Israyeli, okhala mwa Akanani, adzakhala naco colowa cao mpaka pa Zarefati; ndi andende a ku Yerusalemu okhala m'Sefaradi adzakhala nayo midzi ya kumwela, colowa cao.
21. Ndipo apulumutsi adzakwera pa phiri la Ziyoni kuweruza phiri la Esau; ndipo ufumu udzakhala wace wa Yehova.