1. Ha, mapazi ako akongola m'zikwakwata,Mwana wamkaziwe wa mfumu!Pozinga m'cuuno mwako pakunga zonyezimira,Nchito ya manja a mmisiri waluso.
2. Pamcombo pako pakunga cikho coulungika,Cosasowamo vinyo wosanganika:Pamimba pako pakunga mulu wa tiriguWozingidwa ndi akakombo.
3. Maere ako akunga ana awiri a nswalaAnabadwa limodzi.
4. Khosi lako likunga nsanja yaminyanga;Maso ako akunga matawale a ku Hesiboni,A pa cipata ca Batirabimu;Mphuno yako ikunga nsanja ya ku LebanoImene iloza ku Damasiko.
5. Mutu wako ukunga Karimeli,Ndi tsitsi la pamtu pako likunga nsaru yakuda;Mfumu yamangidwa ndi nkhata zace ngati wamsinga.
6. Ha, ndiwe wokongola ndi wofunika,Bwenziwe, m'zokondweretsa!
7. Msinkhu wakowu ukunga mlaza,Maere ako akunga matsango amphesa,
8. Ndinati, Ndikakwera pamlazapo,Ndikagwira nthambi zace:Maere ako ange ngati matsango amphesa,Ndi kununkhira kwa mpweya wako ngati maula;
9. M'kamwa mwako munge ngati vinyo woposa,Womeza tseketeke bwenzi langa,Wolankhulitsa milomo ya ogona tulo.
10. Ndine wa wokondedwa wanga mnyamatayo,Ndine amene andifunayo.
11. Tiye, bwenzi langa, tinke kuminda;Titsotse m'miraga.
12. Tilawire kunka ku minda yamipesa;Tiyang'ane ngati mpesa waphuka, kunje ndi kuonetsa zipatso,Makangaza ndi kutuwa maluwa ace;Pompo ndidzakupatsa cikondi canga,
13. Mandimu anunkhira,Ndi pamakomo pathu zipatso zabwino, za mitundu mitundu, zakale ndi zatsopano,Zimene ndakukundikira iwe, wokondedwa wanga.