Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nyimbo 2 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndine duwa lofiira la ku Saroni,Ngakhale kakombo wa kuzigwa.

2. Ngati kakombo pakati pa mingaMomwemo wokondedwa wanga pakati pa ana akazi.

3. Ngati maula pakati pa mitengo ya m'nkhalango,Momwemo wokondedwa wanga pakati pa ana amuna.Ndinakondwa pakukhala pa mthunzi wace,Zipatso zace zinatsekemera m'kamwa mwanga.

4. Anandifikitsa ku nyumba ya vinyo,Mbendera yace yondizolimira inali cikondi.

5. Mundilimbikitse ndi mphesa zouma, munditonthoze mtima ndi maula,Pakuti ndadwala ndi cikondi.

6. Dzanja lace lamanzere anditsamiritse kumutu,Dzanja lace lamanja ndi kundifungatira.

7. Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu,Pali mphoyo, ndi nswala za kuthengo,Kuti musautse, ngakhale kugalamutsa cikondi,Mpaka cikafuna mwini.

8. Mau a wokondedwa wanga mnyamatayo! Taona, adza,Alikulumpha pamapiri, alikujidimuka pazitunda.

9. Wokondedwa wanga akunga mphoyo, pena mwana wa mbawala:Taona, aima patseri pa khoma pathu,Apenyera pazenera, Nasuzumira pamade.

10. Wokondedwa wanga analankhula, nati kwa ine,Tauka, bwenzi langa, wokongola wanga, tiye.

11. Pakuti, taona, cisanu catha,Mvula yapita yaleka;

12. Maluwa aoneka pansi;Nthawi yoyimba mbalame yafika,Mau a njiwa namveka m'dziko lathu;

13. Mkuyu uchetsa nkhuyu zace zosakhwima,Mipesa niphuka,Inunkhira bwino.Tauka, bwenzi langa, wokongola wangawe, tiyetu.

14. Nkhunda yangawe, yokhala m'ming'alu ya thanthwe, mobisika motsetsereka,Ndipenye nkhope yako, ndimve manako;Pakuti mau ako ngokoma, nkhope yako ndi kukongola.

15. Mutigwirire ankhandwe, ngakhale ang'ono, amene akuononga minda yamipesa;Pakuti m'minda yathu yamipesa muphuka biriwiri.

16. Wokondedwa wanga ndi wa ine, ine ndine wace:Aweta zace pakati pa akakombo,

17. Mpaka dzuwa litapepa, mithunzi ndi kutanimpha,Bwera, bwenzi langawe, nukhale ngati mphoyo pena mwana wa mbawalaPa mapiri a mipata.