Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nyimbo 4:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Taona, wakongola, bwenzi langa, namwaliwe, taona, wakongola;Maso ako akunga a nkhunda patseri pa cophimba cako:Tsitsi lako likunga gulu la mbuzi,Zooneka pa phiri la Gileadi.

2. Mano ako akunga gulu la nkhosa zosengasenga,Zokwera kucokera kosamba;Yonse iri ndi ana awiri,Palibe imodzi yopoloza.

3. Milomo yako ikunga mbota yofiira,M'kamwa mwako ndi kukoma:Palitsipa pako pakunga phande la khangazaPatseri pa cophimba cako.

4. Khosi lako likunga nsanja ya Davide anaimangira zida,Apacikapo zikopa zikwi,Ngakhale zikopa zonse za amuna amphamvu,

5. Maere ako awiri akunga ana awiri a nswala obadwa limodzi,Akudya pakati pa akakombo.

6. Mpaka dzuwa litapepa, mithunzi ndi kutanimpha,Ndikamuka ku phiri la nipa,Ndi ku citunda ca mtanthanyerere.

Werengani mutu wathunthu Nyimbo 4