Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 8:12-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo Alevi aike manja ao pa mitu ya ng'ombezo; pamenepo ukonze imodzi ikhale nsembe yaucimo, ndi inzace, nsembe yopsereza za Yehova, kucita cotetezera Alevi.

13. Ndipo uimike Alevi pamaso pa Aroni, ndi pamaso pa ana ace, ndi kuwapereka ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.

14. Momwemo upatule Alevi mwa ana a Israyeli; kuti Alevi akhale anga.

15. Ndipo atatero alowe Alevi kucita Debito ya cihema cokomanako; ndipo uwayeretse, ndi kuwapereka ngati nsembe yoweyula.

16. Pakuti aperekedwa konse kwa Ine ocokera mwa ana a Israyeli; ndadzitengera iwo m'malo mwa onse akutsegula m'mimba, ndiwo oyamba kubadwa a ana a Israyeli.

17. Pakuti a oyamba kubadwa onse mwa ana a Israyeli ndi anga, mwa anthu ndi zoweta; tsiku lija ndinakantha oyamba kubadwa onse m'dziko la Aigupto, ndinadzipatulira iwo akhale anga.

18. Ndipo ndatenga Alevi m'malo mwa oyamba kubadwa onse mwa ana a Israyeli.

19. Ndipo ndapereka Alevi akhale mphatso ya kwa Aroni ndi ana ace amuna yocokera mwa ana a Israyeli, kucita nchito ya ana a Israyeli, m'cihema cokomanako ndi kucita cotetezera ana a Israyeli; kuti pasakhale mliri pakati pa ana a Israyeli, pakuyandikiza ana a Israyeli ku malo opatulika.

Werengani mutu wathunthu Numeri 8