Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 22:36-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Pamene Balaki anamva kuti wafika Balamu, anamturukira kukakomana naye ku mudzi wa Moabu, wokhala m'mphepete mwa Arinoni, ndiwo ku malekezero a malire ace.

37. Ndipo Balaki anati kwa Balamu, Kodi sindinatumiza kwa iwe ndithu kukakuitana? Unalekeranji kudza kwa ine? sindikhoza kodi kukucitira ulemu?

38. Ndipo Balamu anati kwa Balaki, Taonani, ndafika kwa inu; ngati ndiri nayo mphamvu konse tsopano kunena kanthu? mau amene Mulungu aike m'kamwa mwanga ndiwo ndidzanena.

39. Ndipo Balamu anamuka ndi Balaki, nafika iwo ku Kiriyati Huzoti.

40. Pamenepo Balaki anapha ng'ombe ndi nkhosa, natumizira Balamu, ndi akalonga okhala naye.

41. Ndipo kunali kuti m'mawa, Balaki anatenga Balamu, nakwera nave ku misanje ya Baala, ndi kumeneko anaona malekezero a anthuwo.

Werengani mutu wathunthu Numeri 22