Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 20:6-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo Mose ndi Aroni anacoka pamaso pa msonkhano kumka ku khomo la cihema cokomanako, nagwa nkhope zao pansi; ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera iwo.

7. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

8. Tenga ndodoyo, nusonkhanitse khamulo; iwe ndi Aroni mbale wako, munene ndi thanthwe pamaso pao, kuti liwapatse madzi; potero uwaturutsire madzi m'thanthwe, ndi kumwetsa khamu la anthu ndi zoweta zao.

9. Ndipo Mose anatenga ndodoyo kuicotsa pamaso pa Yehova, monga iye anamuuza iye.

10. Ndipo Mose ndi Aroni anasonkhanitsa msonkhano pathanthwe, nanena nao iye, Tamvanitu, opikisana naye inu; kodi tikuturutsireni madzi m'thanthwe umu?

11. Ndipo Mose anasamula dzanja lace, napanda thanthwe kawiri ndi ndodo; ndipo madzi anaturukamo ocuruka, ndi khamulo linamwa, ndi zoweta zao zomwe.

12. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, Popeza simunandikhulupirira Ine, kundipatula Ine pamaso pa ana a Israyeli, cifukwa cace simudzalowetsa msonkhano uwu m'dziko ndinawapatsali.

13. Awa ndi madzi a Meriba; popeza ana a Israyeli anatsutsana ndi Yehova, ndipo anapatulidwa mwa iwowa.

14. Pamenepo Mose anatumiza amithenga ocokera ku Kadesi kumuka kwa mfumu ya Edomu, ndi kuti, Atero mbale wanu Israyeli, Mudziwa zowawa zonse zinatigwera;

Werengani mutu wathunthu Numeri 20