Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 20:14-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Pamenepo Mose anatumiza amithenga ocokera ku Kadesi kumuka kwa mfumu ya Edomu, ndi kuti, Atero mbale wanu Israyeli, Mudziwa zowawa zonse zinatigwera;

15. kuti makolo athu anatsikira kumka ku Aigupto, ndipo tinakhala m'Aigupto masiku ambiri; ndipo Aaigupto anacitira zoipa ife, ndi makolo athu.

16. Pamenepo tinapfuulira kwa Yehova, ndipo anamva mau athu, natuma mthenga, natiturutsa m'Aigupto; ndipo, taonani, tiri m'Kadesi, ndiwo mudzi wa malekezero a malire anu.

17. Tipitetu pakati pa dziko lanu; sitidzapitira pamunda, kapena munda wampesa, sitidzamwa madzi a m'zitsime; tidzatsata mseu wacifumu; sitidzapatukira kulamanja kapena kulamanzere, mpaka titapitirira malire anu.

18. Koma Edomu ananena naye, Usapitire pakati pa ine, kuti ndingaturuke kukomana nawe ndi lupanga.

19. Ndipo ana a Israyeli ananena naye, Tidzatsata mseu; ndipo tikakamwa madzi ako, ine ndi zoweta zanga, pamenepo ndidzapatsa mtengo wace; sindifuna kanthu kena koma kungopitapo mwa njira.

20. Koma anati, Usapitirepo. Ndipo Edomu anaturukira kukumana naye ndi anthu ambiri, ndi dzanja lamphamvu.

21. Potero Edomu anakana kulola Israyeli kupitira pa malire ace; cifukwa cace Aisrayeli anampatukira.

22. Ndipo anayenda ulendo kucokera ku Kadesi; ndi ana a Israyeli, ndilo khamu lonse, anadza ku phiri la Hori.

23. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni m'phiri la Hori, pa malire a dziko la Edomu, ndi kuti,

24. Aroni adzaitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wace; pakuti sadzalowa m'dziko limene ndapatsa ana a Israyeli, popeza munapikisana ndi mau anga ku madzi a Meriba.

Werengani mutu wathunthu Numeri 20