Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 7:1-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo atatha kumanga linga, ndinaika zitseko, nakhazika odikira, ndi oyimbira, ndi Alevi;

2. ndipo ndinawapatsa mbale wanga Hanani, ndi Hananiya kazembe wa kuboma, ulamuliro wa pa Yerusalemu; popeza ndiye munthu wokhulupirika, naposa ambiri pakuopa Mulungu.

3. Ndinanenanso nao, Asatsegule pa zipata za Yerusalemu lisanafunde dzuwa; ndi poimirira odikira atseke pazipata, nimuzipiringidze, nimuike alonda mwa iwo okhala m'Yerusalemu, yense polindirira pace, yense pandunji pa nyumba yace.

4. Mudziwo tsono ndi wacitando, ndi waukuru; koma anthu anali m'mwemo ngowerengeka, nyumba zomwe sizinamangike.

5. Ndipo Mulungu wanga anaika m'mtima mwanga kuti ndiwasonkhanitse aufuru, ndi olamulira, ndi anthu, kuti awerengedwe mwa cibadwidwe cao. Ndipo ndinapeza buku la cibadwidwe la iwo adakwerako poyamba paja; ndinapeza mudalembedwa m'mwemo.

6. Ana a dziko amene anakwera kucokera kundende a iwo adatengedwa ndende, amene Nebukadinezara mfumu ya Babulo adawatenga, anabwera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, yense ku mudzi wace, ndi awa:

7. ndiwo amene anadza ndi Zerubabele: Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Moredekai, Bilisani, Misiperete, Bigivai, Nehumu, Baana. Mawerengedwe a amuna a anthu Aisrayeli ndiwo:

8. ana a Parosi zikwi ziwiri mphambu zana limodzi kudza makumi asanu ndi awiri.

9. Ana a Sefatiya, mazana atatu mphambu makumi asanu ndi awiri kudza awiri.

10. Ana a Ara, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu kudza awiri.

11. Ana a Pakati Moabu, a ana a Yesuwa ndi Yoabu, zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi atatu kudza khumi limodzi ndi asanu ndi atatu.

12. Ana a Elamu, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri ndi makumi asanu kudza anai.

13. Ana a Zatu, mazana asanu ndi atatu mphambu makumi anai kudza asanu.

14. Ana a Zakai, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi asanu ndi limodzi.

15. Ana a Binui, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi anai kudza asanu ndi atatu.

16. Ana a Betai, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 7