Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 12:30-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Ndipo ansembe ndi Alevi anadziyeretsa okha, nayeretsa anthu, ndi zipata, ndi linga.

31. Pamenepo ndinakwera nao akuru a Yuda pa lingali, ndinaikanso oyamikira magulu awiri akuru oyenda molongosoka; lina loyenda ku dzanja lamanja palinga kumka ku cipata ca kudzala;

32. ndi pambuyo pao anayenda Hosaya, ndi limodzi la magawo awiri a akuru a Yuda,

33. ndi Azariya, Ezara ndi Mesulamu,

34. Yuda, ndi Benjamini, ndi Semaya, ndi Yeremiya,

35. ndi ana ena a ansembe ndi malipenga: Zekariya mwana wa Yonatani, mwana wa Semaya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mikaya, mwana wa Zakuri, mwana wa Asafu,

36. ndi abale ace: Semaya, ndi Azareli, Milalai, Gilelai, Maai, Netaneli, ndi Yuda, Hanani, ndi zoyimbira za Davide munthu wa Mulungu; ndi Ezara mlembiyo anawatsogolera;

37. ndi ku cipata ca kucitsime, ndi kundunji kwao, anakwerera pa makwerero a mudzi wa Davide, potundumuka linga, popitirira pa nyumba ya Davide, mpaka ku cipata ca kumadzi kum'mawa.

38. Ndi gulu lina la oyamikira linamuka mokomana nao, ndi ine ndinawatsata, pamodzi ndi limodzi la magawo awiri la anthu palinga, napitirira pa nsanja ya ng'anjo, mpaka ku linga lacitando;

39. ndi pamwamba pa cipata ca Efraimu, ndi ku cipata cakale, ndi ku cipata cansomba, ndi nsanja ya Hananeli, ndi nsanja ya Hameya, mpaka ku cipata cankhosa; ndipo anaima ku cipata cakaidi.

40. Atatero, magulu awiriwo a iwo oyamikira anaima m'nyumba ya Mulungu, ndipo ine ndi limodzi la magawo awiri a olamulira pamodzi ndi ine;

41. ndi ansembe, Eliakimu, Maaseya, Minyamini, Mikaya, Elioenai, Zekariya, ndi Hananiya, ali nao malipenga;

42. ndi Maaseya, ndi Semaya, ndi Eleazara, ndi Uzi, ndi Yehohanana, ndi Malikiya, ndi Elamu, ndi Ezeri. Ndipo oyimbira anayimbitsa Yeziraya ndiye woyang'anira wao.

43. Ndipo anaphera nsembe zambiri tsiku lija, nasekerera; pakuti Mulungu anawakondweretsa ndi cimwemwe cacikuru; ndi akazi omwe ndi ana anakondwera; ndi cikondwerero ca Yerusalemu cinamveka kutali.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 12