Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 11:13-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. ndi abale ace akulu a nyumba za makolo awiri mphambu makumi anai kudza awiri, ndi Amasai mwana wa Azareli, mwana wa Azai, mwana wa Mesilimoti, mwana wa Imeri;

14. ndi abale ao, ngwazi zamphamvu, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu; ndi woyang'anira wao ndiye Zabidiyeli mwana wa Hagedolimu.

15. Ndi mwa Alevi: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni;

16. ndi Sabetai, ndi Yozabadi, mwa akuru a Alevi, anayang'anira nchito za pabwalo za nyumba ya Mulungu;

17. ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu, ndiye mkuru wakuyamba mayamiko, popemphera; ndi Bakibukiya wotsatana naye mwa abale ace, ndi Abida mwana wa Samua, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.

18. Alevi onse m'mudzi wopatulikawo ndiwo mazana awiri mphambu makumi asanu ndi atatu kudza anai.

19. Ndi odikira: Akubu, Talimoni, ndi abale ao akulindira pazipata, ndiwo zana limodzi mphambu makumi asanu ndi awiri kudza awiri.

20. Ndi Aisrayeli otsala, ndiwo ansembe ndi Alevi, anakhala m'midzi yonse ya Yuda, yense m'colowa cace.

21. Koma Anetini anakhala m'Ofeli, ndi Ziya, ndi Gisipa anali oyang'anira Anetini.

22. Ndipo woyang'anira wa Alevi m'Yerusalemu ndiye Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika; mwa ana a Asafu oyimbira ena anayang'anira nchito ya m'nyumba ya Mulungu.

23. Pakuti mfumu inalamulira za iwowa, naikira oyimbira cowathandiza, yense cace pa tsiku lace.

24. Ndi Petatiya mwana wa Mesezabele, wa ana a Zera, mwana wa Yuda, anatumikira mfumu pa mirandu yonse ya anthuwo.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 11