Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mika 7:6-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Pakuti mwana wamwamuna apeputsa atate, mwana wamkazi aukira amace, mpongozi aukira mpongozi wace; adani ace a munthu ndiwo a m'nyumba yace.

7. Koma ine, ndidzadikira Yehova; ndidzalindirira Mulungu wa cipulumutso canga; Mulungu wanga adzandimvera.

8. Usandiseka, mdani wangawe; pakugwa ine ndidzaukanso; pokhala ine mumdima Yehova adzakhala kuunika kwanga.

9. Ndidzasenza mkwiyo wa Yehova, cifukwa ndamcimwira, mpaka andinenera mlandu wanga, ndi kundiweruzira mlandu wanga; adzanditurutsira kwa kuunika, ndipo ndidzapenya cilungamo cace.

10. Pamenepo mdani wanga adzaciona, ndi manyazi adzamkuta iye amene adati kwa ine, Ali kuti Yehova Mulungu wako? Maso anga adzamuona; tsopano adzampondereza ngati thope la m'miseu.

11. Tsiku lakumanga malinga ako, tsiku lomwelo lembalo lidzacotsedwa kunka kutali.

12. Tsiku lomwelo adzadza kwa iwe, kucokera ku Asuri ndi midzi ya ku Aigupto, kuyambira ku Aigupto kufikira ku Mtsinje, ndi kuyambira kunyanja kufikira kunyanja, ndi kuyambira kuphiri kufikira kuphiri.

13. Koma dziko lidzakhala labwinja cifukwa ca iwo okhalamo, mwa zipatso za macitidwe ao.

14. Mudyetse anthu anu ndi ndodo yanu, nkhosa za colowa canu zokhala pa zokha m'nkhalango pakati pa Karimeli, zidye m'Basana ndi m'Gileadi masiku a kale lomwe.

15. Monga masiku a kuturuka kwako m'dziko la Aigupto ndidzamuonetsa zodabwitsa.

16. Amitundu adzaona nadzacita manyazi ndi mphamvu yao yonse; adzagwira pakamwa, m'makutu mwao mudzagontha.

17. Adzanyambita pfumbi ngati njoka; ngati zokwawa za padziko, adzanjenjemera poturuka m'ngaka mwao; adzafika kwa Yehova Mulungu wao ndi mantha, nadzaopa cifukwa ca iwe.

18. Ndani Mulungu wofanana ndi Inu, wakukhululukira mphulupulu, wakupitirira zolakwa za otsala a colowa cace? sasunga mkwiyo wace ku nthawi yonse popeza akondwera naco cifundo.

19. Adzabwera, nadzaticitira nsoni; adzagonjetsa mphulupulu zathu; ndipo mudzataya zocimwa zao zonse m'nyanja yakuya,

20. Mudzapatsa kwa Yakobo coonadi, ndi kwa Abrahamu cifundo cimene munalumbirira makolo athu kuyambira masiku a kale lomwe.

Werengani mutu wathunthu Mika 7