Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mika 7:12-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Tsiku lomwelo adzadza kwa iwe, kucokera ku Asuri ndi midzi ya ku Aigupto, kuyambira ku Aigupto kufikira ku Mtsinje, ndi kuyambira kunyanja kufikira kunyanja, ndi kuyambira kuphiri kufikira kuphiri.

13. Koma dziko lidzakhala labwinja cifukwa ca iwo okhalamo, mwa zipatso za macitidwe ao.

14. Mudyetse anthu anu ndi ndodo yanu, nkhosa za colowa canu zokhala pa zokha m'nkhalango pakati pa Karimeli, zidye m'Basana ndi m'Gileadi masiku a kale lomwe.

15. Monga masiku a kuturuka kwako m'dziko la Aigupto ndidzamuonetsa zodabwitsa.

16. Amitundu adzaona nadzacita manyazi ndi mphamvu yao yonse; adzagwira pakamwa, m'makutu mwao mudzagontha.

17. Adzanyambita pfumbi ngati njoka; ngati zokwawa za padziko, adzanjenjemera poturuka m'ngaka mwao; adzafika kwa Yehova Mulungu wao ndi mantha, nadzaopa cifukwa ca iwe.

18. Ndani Mulungu wofanana ndi Inu, wakukhululukira mphulupulu, wakupitirira zolakwa za otsala a colowa cace? sasunga mkwiyo wace ku nthawi yonse popeza akondwera naco cifundo.

19. Adzabwera, nadzaticitira nsoni; adzagonjetsa mphulupulu zathu; ndipo mudzataya zocimwa zao zonse m'nyanja yakuya,

20. Mudzapatsa kwa Yakobo coonadi, ndi kwa Abrahamu cifundo cimene munalumbirira makolo athu kuyambira masiku a kale lomwe.

Werengani mutu wathunthu Mika 7