Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mika 5:5-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo ameneyo adzakhala Mtendere; pamene a ku Asuri adzalowa m'dziko lathu, ndi pamene adzaponda m'zinyumba zathu, tidzawaukitsira abusa asanu ndi awiri, ndi akalonga asanu ndi atatu.

6. Ndipo iwo adzatha dziko la Asuri ndi lupanga, ndi dziko la Nimrodi, ndilo polowera pace; ndipo adzatilanditsa kwa a ku Asuri pamene alowa m'dziko lathu, pamene aponda m'kati mwa malire athu.

7. Ndipo otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu, ngati mame ocokera kwa Yehova, ngati mvula paudzu, yosacedwera munthu, yosalindira ana a anthu.

8. Ndipo, otsala a Yakobo adzakhala mwa amitundu, pakati pa mitundu yambiri ya anthu, ngati mkango mwa nyama za kuthengo, ngati msona wa mkango mwa magulu a nkhosa; umenewo ukapitako, upondereza, numwetula, ndipo palibe wakupulumutsa.

9. Dzanja lako likwezeke pamwamba pa iwo akuyambana nawe, ndi adani ako onse aonongeke.

10. Ndipo kudzacitika tsiku ilo, ati Yehova, ndidzaononga akavalo ako m'kati mwako, ndi kutha magareta ako;

11. ndipo ndidzaononga midzi ya m'dziko lako, ndi kupasula malinga ako onse;

12. ndipo ndidzaononga zanyanga za m'dzanja lako; ndipo sudzakhalanso nao alosi;

13. ndidzaononganso mafano ako osema, ndi zoimiritsa zako pakati pako; ndipo sudzalambiranso nchito za manja ako.

14. Ndipo ndidzazula zifanizo zako m'kati mwako, ndi kutha midzi yako.

15. Ndipo ndidzabwezera amitundu osamvera cilango mu mkwiyo waukali.

Werengani mutu wathunthu Mika 5