Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mika 5:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Uzisonkhana tsopano magulu magulu, mwana wamkazi wa magulu iwe; watimangira misasa, adzapanda woweruza wa Israyeli ndi ndodo patsaya.

2. Koma iwe, Betelehemu Efrata, ndiwe wamng'ono kuti ukhale mwa zikwi za Yuda, mwa iwe mudzanditurukira wina wakudzakhala woweruza m'Israyeli; maturukiro ace ndiwo a kale lomwe, kuyambira nthawi yosayamba.

3. Cifukwa cace Iye adzawapereka kufikira nthawi yoti wobalayo wabala; pamenepo otsala a abale ace adzabwera pamodzi ndi ana a Israyeli,

4. Ndipo adzaimirira, nadzadyetsa nkhosa zace mu mphamvu ya Yehova, m'ukulu wa dzina la Yehova Mulungu wace; ndipo iwo adzakhalabe; pakuti pamenepo Iye adzakhala wamkuru kufikira malekezero a dziko lapansi.

5. Ndipo ameneyo adzakhala Mtendere; pamene a ku Asuri adzalowa m'dziko lathu, ndi pamene adzaponda m'zinyumba zathu, tidzawaukitsira abusa asanu ndi awiri, ndi akalonga asanu ndi atatu.

6. Ndipo iwo adzatha dziko la Asuri ndi lupanga, ndi dziko la Nimrodi, ndilo polowera pace; ndipo adzatilanditsa kwa a ku Asuri pamene alowa m'dziko lathu, pamene aponda m'kati mwa malire athu.

Werengani mutu wathunthu Mika 5