Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 6:19-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo Yehova analankhula ndi Mose, nati,

20. Copereka ca Aroni ndi ana ace, cimene azibwera naco kwa Yehova tsiku la kudzozedwa iye ndi ici: limodzi la magawo khumi la efa la ufa wosalala, likhale copereka caufa kosalekeza, nusu lace m'mawa, nusu lace madzulo.

21. Cikonzeke paciwaya ndi mafuta; udze naco cokazinga; copereka caufa cazidutsu ubwere naco, cikhale pfungo lokoma la kwa Yehova.

22. Ndipo wansembe wodzozedwa m'malo mwace, wa mwa ana ace, acite ici; likhale lemba losatha; acitenthe konse kwa Yehova.

23. Ndipo zopereka zaufa zonse za wansembe azitenthe konse; asamazidya.

24. Ndipo Yehova analankhula ndi Mose, nati,

25. Lankhula ndi Aroni ndi ana ace, ndi kuti, Cilamulo ca nsembe yaucimo ndi ici: Pamalo pophera nsembe yopsereza ndipo pophera nsembe yaucimo pamaso pa Yehova; ndiyo yopatulikitsa.

26. Ndipo azidya iyi wansembe amene aipereka cifukwa ca zoipa; aidyere m'malo opatulika, pa bwalo la cihema cokomanako.

27. Ali yense akakhudza nyama yace adzakhala wopatulika; ndipo akawaza mwazi wace wina pa cobvala ciri conse, utsuke cimene adauwazaco m'malo opatulika.

28. Ndipo mphika wadothi umene anaphikamo nyamayi auswe, koma ngati anaiphika mu mphika wamkuwa, atsuke uwu, nautsukuluze ndi madzi.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 6