Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 6:13-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Moto uziyakabe pa guwa la nsembe, wosazima.

14. Ndipo cilamulo ca copereka caufa ndico: ana a Aroni azibwera naco pamaso pa Yehova ku guwa la nsembe.

15. Ndipo atengeko wodzala manja pa ufa wa copereka ca ufa wosalala, ndi pa mafuta ace, ndi libona lonse liri pa copereka caufa, nazitenthe pa guwa la nsembe, zicite pfungo lokoma, ndizo cikumbutso cace ca kwa Yehova.

16. Ndipo cotsalira cace adye Aroni ndi ana ace; acidye copanda cotupitsa m'malo opatulika; pa bwalo la cihema cokomanako acidye.

17. Asaciphike ndi cotupitsa, Ndacipereka cikhale gawo lao locokera pa nsembe zanga zamoto; ndico copatulikitsa, monga nsembe yaucimo, ndi monga nsembe yoparamula.

18. Amuna onse a mwa ana a Aroni adyeko, ndilo lemba losatha la ku mibadwo yanu, ciwacokere ku nsembe zamoto za Yehova; ali yense wakuzikhudza izi adzakhala wapatolika.

19. Ndipo Yehova analankhula ndi Mose, nati,

Werengani mutu wathunthu Levitiko 6