Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 25:23-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo asaligulitse dziko cigulitsire; popeza dzikoli ndi langa; pakuti inu ndinu alendo akugonera ndi Ine.

24. Potero muzilola liomboledwe dziko lonse muli nalo.

25. Mbale wako akasaukira cuma, nakagulitsa cace cace, pamenepo mombolo wace, mbale wace weni weni azidza, naombole cimene mbale wace anagulitsaco.

26. Ndipo munthu akasowa mombolo, koma dzanja lace lacionetsa, nacipeza cofikira kuciombola;

27. pamenepo awerenge zaka za kugulitsa kwace, nabwezere wosulayo zotsalirapo, nabwerere iye ku dziko lace.

28. Koma dzanja lace likapanda kupeza zofikira za kumbwezera, pamenepo cogulitsaco cikhale m'dzanja lace la iye adacigulayo, kufikira caka coliza lipenga; koma caka coliza lipenga cituruke, nabwerere iye ku dziko lace.

29. Munthu akagulitsa nyumba yogonamo, m'mudzi wa m'linga, aiombole cisanathe caka coigulitsa; kufikira kutha caka akhoza kuombola.

30. Ndipo akapanda kuiombola kufikira kutha kwace kwa caka camphumphu, nyumba iri m'mudzi wa m'lingayi idzakhala yace ya iye adaigula yosamcokeranso mwa mibadwo yace; siidzaturuka caka coliza lipenga.

31. Koma nyumba za m'midzi yopanda linga aziyese monga minda ya m'dziko; ziomboledwe, zituruke m'caka coliza lipenga.

32. Kunena za midzi ya Alevi, nyumba za m'midzi yao yao, Alevi akhoza kuziombola nthawi zonse.

33. Ndipo munthu akagula kwa Mlevi, nyumba yogulayo yokhala m'mudzi wace wace, ituruke m'caka coliza lipenga, popeza nyumba za m'midzi ya Alevi ndizo zao zao mwa ana a Israyeli.

34. Koma dambo la podyera pao siligulika; popeza ndilo lao lao kosatha.

35. Ndipo mbale wako akasaukira cuma, ndi dzanja lace lisowa; iwe uzimgwiriziza; akhale nawe monga mlendo wakugonera kwanu.

36. Usamambwezetsa phindu, kapena cioniezero; koma uope Mulungu wako; kuti mbale wako akhale nawe.

37. Musamampatsa ndarama zako polira phindu, kapena kumpatsa zakudya kuti aonjezerepo pocibwezera.

38. Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakuturutsani m'dziko la Aigupto, kukupatsani dziko la Kanani, kuti ndikhale Mulungu wanu.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 25