Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 24:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo ukhale wa Aroni ndi ana ace, audye pamalo popatulika; pakuti auyese wopatulikitsa wocokera ku nsembe zamoto za Yehova; ndilo lemba losatha.

10. Ndipo mwana wamwamuna wa mkazi M-israyeli, atate wace ndiye M-aigupto, anaturuka mwa ana a Israyeli; ndi mwana wamwamuna wa mkazi M-israyeliyo analimbana naye munthu M-israyeli kucigono;

11. ndipo mwana wamwamuna wa mkazi M-israyeli anacitira DZINA mwano, natemberera; ndipo anadza naye kwa Mose. Dzina la mai wace ndiye Selomiti, mwana wa Dibri, wa pfuko la Dani.

12. Ndipo anamsunga m'kaidi, kuti awafotokozere m'mene anenere Yehova.

13. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

Werengani mutu wathunthu Levitiko 24