Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 16:8-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo Aroniayesemaere pa mbuzi ziwirizo; maere amodzi kwa Yehova, ndi amodzi kwa Azazeli.

9. Ndipo Aroni abwere nayo mbuzi imene adaigwera maere a Yehova, naiyese nsembe yaucimo.

10. Koma mbuzi imene adaigwera maere a Azazeli, aiike yamoyo pamaso pa Yehova, kuti acite nayo cotetezera, kuitumiza kucipululu ikhale ya Azazeli.

11. Ndipo Aroni abwere nayo ng'ombe ya nsembe yaucimo, ndiyo yace yace, nadzitetezere iye yekha, ndi mbumba yace, ndi kupha ng'ombe ya nsembe yaucimo ndiyo yace yace;

12. natenge mbale ya zofukiza yodzala ndi makara amoto, kuwacotsa pa guwa la nsembe, pamaso pa Yehova, ndi manja ace odzala ndi cofukiza copera ca pfungo lokoma, nalowe nayo m'tseri mwa nsaru yocinga;

13. naike cofukizaco pamoto pamaso pa Yehova, kuti mtambo wa cofukiza ciphimbe cotetezerapo cokhala pamboni, kuti angafe.

14. Ndipo atengeko mwazi wa ng'ombeyo, ndi kuuwaza ndi cala cace pacotetezerapo, mbali ya kum'mawa; nawaze mwazi ndi cala cace cakuno ca cotetezerapo kasanu ndi kawiri.

15. Pamenepo aiphe mbuzi ya nsembe yaucimo, ndiyo yophera anthu, nalowe nao mwazi wace m'tseri mwa nsaru yocinga, nacite nao mwazi wace monga umo anacitira ndi mwazi wa ng'ombe, nauwaze pacotetezerapo ndi cakuno ca cotetezerapo;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 16