Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 15:8-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo wakukhayo akalabvulira wina woyera; pamenepo atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.

9. Ndipo mbereko iri yonse akwerapo wakukhayo iri yodetsedwa.

10. Ndipo munthu ali yense akakhudza kanthu kali konse kadali pansi pace adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo; ndipo iye wakunyamula zimenezo atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.

11. Ndipo munthu ali yense wakukhayo akamkhudza, osasambatu m'manja m'madzi, atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.

12. Ndipo zotengera zadothi wazikhudza wakukhayo, aziphwanye; ndi zamtengo, azitsuke ndi madzi.

13. Ndipo wakukhayo atayeretsedwa ku kukha kwace, adziwerengere masiku asanu ndi awiri akhale a kuyeretsa kwace, natsuke zobvala zace; nasambe thupi lace ndi madzi oyenda, nadzakhala woyera.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 15