Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 13:38-54 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. Ndipo ngati mwamuna kapena mkazi ali ndi zikanga pa khungu la thupi lace, zikanga zoyerayera;

39. wansembe aziona; ndipo taonani ngati zikanga ziri pa khungu la thupi lao zikhala zotuwatuwa; ndilo thuza labuka pakhungu; ndiye woyera.

40. Ndipo ngati tsitsi la munthu lathothoka, ndiye wadazi; koma woyera.

41. Ndipo ngati tsitsi lathothoka pamphumi pace ndiye wa masweswe, koma woyera.

42. Koma ngati pali nthenda yotuuluka pakati pa dazi lace la pamutu, kapena la pamphumi, ndipo khate lirikubuka pakati pa dazi lace la pamutu, kapena la pamphumi.

43. Pamenepo wansembe azimuona, ndipo taonani, ngati cotupa cace ca nthenda ciri cotuuluka pa dazi la pa mutu wace, kapena la pamphumi pace, monga maonekedwe a khate pa khungu la thupi;

44. ndiye wakhate, ndiye wodetsedwa; wansembe amuchetu wodetsedwa; nthenda yace iri pamutu pace.

45. Ndipo azing'amba zobvala zace za wakhate ali ndi nthendayo, ndi tsitsi la pamutu pace lizikhala lomasuka, naphimbe iye mlomo wace wa m'mwamba, napfuule, Wodetsedwa, wodetsedwa!

46. Masiku onse nthenda ikali pa iye azikhala wodetsedwa; ali wodetsedwa, agone pa yekha pokhala pace pakhale kunja kwa cigono.

47. Ndiponso ngati nthenda yakhate iri pa cobvala caubweya, kapena cathonje;

48. ngakhale iri pamuyaro, kapena pamtsendero, cathonje, kapena caubweya, ngakhale iri pa cikopa, kapena pa cinthu ciri conse copanga ndi cikopa;

49. ngati nthenda iri yobiriwira, kapena yofiira pacobvala, kapena pacikopa, kapena pamuyaro, kapena pamtsendero, kapena pa cinthu ciri conse copangika ndi cikopa, ndiyo nthenda yakhate; aziionetsa kwa wansembe;

50. ndipo wansembe aone nthendayo, nabindikiritse ciija ca nthenda masiku asanu ndi awiri;

51. naone nthenda tsiku lacisanu ndi ciwiri; ngati nthenda yakula pacobvala, ngakhale pamuyaro, kapena pamtsendero, kapena pacikopa, ziri zonse zanchito zopangika ndi cikopa; nthendayo ndiyo khate lofukuta; ndico codetsedwa.

52. Ndipo atenthe cobvalaco ngakhale muyaro wace, ngakhale mtsendero wace, caubweya kapena cathonje, kapena ciri conse cacikopa ciri ndi khate, ndilo khate lofetsa; acitenrhe ndi mote.

53. Ndipo wansembe akaona, ndipo taonani, nthenda njosakula pacobvala, kapena pamuyaro, kapena pamtsendero, kapena pa cinthu ciri conse copangika ndi cikopa;

54. pamenepo wansembe aziuza kuti atsuke cija pali khate, nacibindikiritse masiku asanu ndi awiri ena;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 13