Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 13:27-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. ndipo wansembe amuone tsiku lacisanu ndi ciwiri; ngati cakula pakhungu, wansembe amuche wodetsedwa; ndiyo nthenda yakhate,

28. Ndipo ngati cikanga ciima pomwepo, cosakula pakhungu koma cazimba; ndico cotupa ca kupsya; ndipo wansembe amuche woyera; pakuti ndico cipsera ca kupsya.

29. Ndipo ngati mwamuna kapena mkazi ali ndi nthenda pamutu kapena pandebvu,

30. wansembe aziona nthenda; ndipo taonani, ngati ioneka yokumba kubzola khungu, ndipo pali tsitsi loyezuka lotetemera; pamenepo wansembe amuche wodetsedwa; ndiyo mfundu, ndilo khate la mutu kapena ndebvu.

31. Ndipo wansembe akaona nthenda yamfundu, ndipo taonani, ioneka yosakumba kubzola khungu, ndipo palibe tsitsi lakuda pamenepo, wansembe ambindikiritse iye ali ndi mfundu masiku asanu ndi awiri;

32. ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri wansembe aone nthendayi; ndipo taonani, ngati mfundu njosakula, ndipo mulibe tsitsi loyezuka, ndipo mfundu ikaoneka yosakumba kubzola khungu,

33. pamenepo azimeta, koma osameta pamfundu; ndipo wansembe ambindikiritse iye wamfundu masiku asanu ndi awiri ena;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 13