Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 1:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. NDIPO Yehova anaitana Mose, nanena naye ali m'cihema cokomanako iye, nati,

2. Lankhula ndi ana a lsrayeli, nunene nao, Ali yense mwa inu akabwera naco copereka ca kwa Yehova, muzibwera naco copereka canu cikhale ca zoweta, ca ng'ombe, kapena ca nkhosa, kapena ca mbuzi.

3. Copereka cace cikakhala nsembe yopsereza ya ng'ombe, azibwera nayo yaimuna yopanda cirema; abwere nayo ku khomo la cihema cokomanako, kuti alandirike pamaso pa Yehova.

4. Ndipo aike dzanja lace pamutu pa nsembe yopsereza; ndipo idzalandiridwa m'malo mwace, imtetezere.

5. Pamenepo aiphe ng'ombeyo pamaso pa Yehova; ndipo ana a Aroni, ansembewo, abwere nao mwazi, nawaze mwaziwo pozungulira pa guwa la nsembe, lokhala pa khoma la cihema cokomanako.

6. Ndipo asende nsembe yopsereza, ndi kuikadzula ziwalo zace.

7. Ndipo ana a Aroni asonkhe mota pa guwa la nsembe, ndi kukonza nkhuni pamotopo;

8. ndi ana a Aroni, ansembewo, akonze ziwalozo, mutu, ndi mafuta pa nkhuni ziri pa mota wa pa guwa la nsembe;

Werengani mutu wathunthu Levitiko 1