Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 7:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. M'mene ndiciritsa Israyeli, mphulupulu ya Efraimu ibvumbuluka, ndi zoipa za Samariya; pakuti acita bodza, ndipo mkhungu alowa m'nyumba, ndi gulu la mbala manca kubwalo.

2. Ndipo sanena m'mtima mwao kuti Ine ndikumbukila zoipa zao zonse; tsopano macitidwe ao awazinga; ali pamaso panga,

3. Akondweretsa mfumu ndi zoipa zao, ndi akalonga ndi mabodza ao.

4. Acigololo onsewo; akunga ng'anjo anaitenthetsa wooca mkate; aleka kusonkha moto, poyambira kukanda mtanda kufikira watupa mtandawo.

5. Tsiku la mfumu yathu akalonga adzidwalitsa ndi kutentha kwa vinyo; iye anatambasula dzanja lace pamodzi ndi oseka.

6. Pakuti asendera nao mtima wao wakunga ng'anjo ya mkate, pokhala alikulalira; wooca mkate wao agona usiku wonse, m'mawa iyaka ngati moto wa malawi.

7. Onsewo atentha ngati ng'anjo, natha oweruza ao, agwa mafumu ao onse; palibe mmodzi mwa iwo wakuitana Ine.

8. Efraimu asokonezana nayo mitundu ya anthu; Efraimu ndiye kamtanda ka mkate kosatembenuzidwa.

9. Alendo anatha mphamvu yace osacidziwaiye; imvi zomwe zampakiza osacidziwa iye,

10. Ndipo kudzikuza kwa Israyeli kumcitira umboni pamaso pace; koma sanabwerera kumka kwa Yehova Mulungu wao, kapena kumfunafuna mwa ici conse.

11. Ndipo Efraimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru; aitanira kwa Aigupto, amuka kwa Asuri.

12. Pamene amuka ndidzawayalira ukonde wanga, ndidzawagwetsa ngati mbalame za m'mlengalenga, ndidzawalanga monga udamva msonkhano wao.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 7