Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 41:5-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo anagona nalotanso kaciwiri: ndipo taonani, ngala zisanu ndi ziwiri za tirigu zinamera pa mbuwa imodzi, zonenepa ndi zabwino.

6. Ndipo, taonani, ngala zisanu ndi ziwiri, zoonda zopsyerera ndi mphepo ya kum'mawa, zinamera pambuyo pao.

7. Ndipo ngala zoondazo zinameza ngala zisanu ndi ziwiri zonenepa ndi zodzalazo. Ndipo Farao anauka, ndipo, taonani, analota.

8. Ndipo panali m'mamawa mtima wace unabvutidwa; ndipo anatumiza naitana amatsenga onse a m'Aigupto, ndi anzeru onse a momwemo: ndipo Farao anafotokozera iwo loto lace; koma panalibe mmodzi anakhoza kuwamasulira iwo kwa Farao.

9. Pamenepo wopereka cikho wamkuru anati kwa Farao, kuti, Ine ndidzakumbukira zocimwa zanga lero.

10. Farao anakwiya ndi anyamata ace, nandiika ine ndisungidwe m'nyumba ya kazembe wa alonda, ine ndi wophika mkate wamkuru:

11. ndipo tinalota loto usiku umodzi ine ndi iye; tinalota munthu yense monga mwa kumasulira kwa loto lace.

12. Ndipo panali ndi ife mnyamata, Mhebri, kapolo wa kazembe wa alonda, ndipo ife tinafotokozera iye, ndipo iye anatimasulira ife maloto athu; kwa munthu yense monga mwa loto lace anatimasulira.

13. Ndipo panali monga momwe iye anatimasulira, momwemo mudacitika; ine anandibwezera mu utumiki wanga, mnzanga anampacika.

14. Ndipo Farao anatumiza nakaitana Yosefe; ndipo anamturutsa iye msanga m'dzenjemo: ndipo iye anameta, napindula malaya ace, nalowa kwa Farao.

Werengani mutu wathunthu Genesis 41