Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 36:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mibadwo ya Esau (ndiye Edomu) ndi iyi:

2. Esau anatenga akazi ace a ana akazi a m'Kanani: Ada mwana wamkazi wa Eloni Mhiti, ndi Oholibama mwana wamkazi wa Ana, mwana wamkazi wa Zibeoni Mhivi;

3. ndi Basemati mwana wamkazi wa lsmayeli, mlongo wace wa Nabayoti.

4. Ndipo Ada anambalira Esau Elifazi; ndipo Basemati anabala Reueli;

5. ndipo Oholibama anabala Jeusi, ndi Jalamu, ndi Kora; amenewa ndi ana amuna a Esau, amene anambadwira m'dziko la Kanani.

6. Ndipo Esau anatenga akazi ace, ndi ana ace amuna, ndi ana ace akazi, ndi anthu onse a m'banja mwace, ndi ng'ombe zace, ndi zoweta zace, ndi zonse anali nazo anasonkhanitsa m'dziko la Kanani; ndipo ananka ku dziko losiyana patari ndi Yakobo mphwace.

7. Cifukwa cuma cao cinali cambiri cotero kuti sanakhoza kukhala pamodzi; ndipo dziko lokhalamo iwo silinakhoza kuwakwanira cifukwa ca ng'ombe zao.

8. Ndipo Esau anakhala m'phiri la Seiri; Esau ndiye Edomu.

9. Mibadwo ya Esau atate wao wa Aedomu m'phiri la Seiri ndi iyi:

10. amenewa ndi maina a ana amuna a Esau: Elifazi mwana wamwamuna wa Ada, mkazi wace wa Esau, Reueli mwana wamwamuna wa Basemati mkazi wace wa Esau.

11. Ndipo ana amuna a Elifazi ndiwo Temani, Omari, Zefo ndi Gatamu, ndi Kenazi.

12. Ndipo Timna anali mkazi wace wamng'ono wa Elifazi mwana wamwamuna wa Esau; ndipo anambalira Elifazi Amaleki: amenewa ndi ana amuna a Ada mkazi wace wa Esau.

Werengani mutu wathunthu Genesis 36