Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 30:1-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamene Rakele anaona kuti sanambalira Yakobo ana, Rakele anamcitira mkuru wace nsanje; nati kwa Yakobo, Ndipatse ana ndingafe.

2. Ndipo Yakobo anapsa mtima ndi Rakele; nati, Kodi ine ndikhala m'malo a Mulungu amene akukaniza iwe zipatso za mimba?

3. Ndipo Rakele anati, Taonani mdzakazi wanga Biliha, mulowe kwa iye; ndipo iye adzabala pa maondo anga, kuti inenso ndionerepo ana pa iye.

4. Ndipo Rakele anampatsa iye Biliha mdzakazi wace akhale mkazi wace; ndipo Yakobo analowa kwa iye.

5. Ndipo Biliha anatenga pakati, nambalira Yakobo mwana wamwamuna.

6. Rakele ndipo anati, Mulungu wandiweruzira ine, namva mau anga, nandipatsa ine mwana; cifukwa cace anamucha dzina lace Dani.

7. Ndipo Biliha mdzakazi wace wa Rakele anatenganso pakati, nambalira Yakobo mwana wamwamuna waciwiri.

8. Ndipo Rakele anati, Ndi malimbano a Mulungu ndalimbana naye mkuru wanga, ndipo ndapambana naye; ndipo anamucha dzina lace Nafitali.

9. Pamene Leya anaona kuti analeka kubala, anatenga Zilipa mdzakazi wace, nampatsa iye kwa Yakobo kuti akhale mkazi wace.

10. Ndipo Zilipa mdzakazi wace wa Leya anambalira Yakobo mwana wamwamuna.

11. Ndipo Leyaanati, Wamwai ine! ndipo anamucha dzina lace Gadi.

12. Ndipo Zilipa mdzakazi wa Leya anambalira Yakobo mwana wamwamuna waciwiri.

13. Ndipo Leya anati, Ndakondwa inel cifukwa kuti ana akazi adzandicha ine wokondwa: ndipo anamucha dzina lace Aseri.

Werengani mutu wathunthu Genesis 30