Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 25:17-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Zaka za moyo wa Ismayeli ndi izi: zaka zana limodzi kudza makumi atatu ndi zisanu ndi ziwiri: ndipo iye anamwalira, natengedwa akhale ndi a mtundu wace.

18. Ndipo anakhala iwo kuyambira ku Havila kufikira ku Suri, ndiko kum'mawa kwace kwa Aigupto, pakunka ku Asuri: ndipo iye anakhala pamaso pa abale ace onse.

19. Mibadwo ya Isake mwana wace wa Abrahamu ndi iyi: Abrahamu anabala Isake:

20. ndipo Isake anali wa zaka makumi anai pamene anakwata Rebeka, mwana wamkazi wa Betuele Msuriya wa ku Padanaramu, mlongo wace wa Labani Msuriya.

21. Ndipo Isake anampembedzera mkazi wace kwa Yehova popeza anali wouma: ndipo Yehova analola kupembedza kwace, ndipo Rebeka mkazi wace anatenga pakati,

22. Ndipo ana analimbana m'kati mwace: ndipo iye anati, Ngati cotero, ine ndikhala ndi moyo bwanji? ndipo ananka kukafunsa kwa Yehova.

23. Yehova ndipo anati kwa iye,Mitundu iwiri iri m'mimba mwako,Magulu awiri a anthu adzaturuka m'mimba mwako;Gulu lina lidzapambana mphamvu ndi linzace;Wamkuru adzakhala kapolo wa wamng'ono.

24. Atatha masiku ace akubala, taonani, amapasa anali m'mimba mwace.

25. Ndipo woyamba anabadwa wofiira, monse mwace monga maraya aubweya; ndipo anamucha dzina lace Esau.

26. Pambuyo pace ndipo anabadwa mphwace ndipo dzanja lace linagwira citende ca Esau, ndi dzina lace linachedwa Yakobo: ndipo Isake anali wa zaka makumi asanu ndi limodzi pamene mkazi wace anabala iwo.

27. Ndipo anakula anyamatawo; ndipo Esau anali munthu wakudziwa zakusaka nyama, munthu wa m'thengo; ndipo Yakobo anali munthu wofatsa, wakukhala m'mahema.

28. Ndipo Isake anakonda Esau, cifukwa anadya nyama yace ya m'thengo; koma Rebeka anakonda Yakobo,

29. Ndipo Yakobo anaphika mphodza: ndipo Esau anacokera kuthengo, nalefuka:

30. ndipo Esau anati kwa Yakobo, Undipatse ndidye cofiiraco; cifukwa ndalefuka: cifukwa cace anamucha dzina lace Edomu.

31. Ndipo Yakobo anati, Tigulane lero ukulu wako.

Werengani mutu wathunthu Genesis 25