Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 24:49-60 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

49. Tsopano, ngati mudzamcitira mbuyanga zaufulu ndi zoonadi, mundiuze, ngati iai, mundiuze; kuti ndipatukire ku dzanja lamanja kapena ku dzanja lamanzere.

50. Ndipo anayankha Labani ndi Betuele, nati, Caturuka kwa Yehova cinthu ici; sitingathe kunena ndi iwe coipa kapena cabwino.

51. Taonani, Rebeka ali pamaso pako, mtenge ndi kumuka, akhale mkazi wa mwana wa mbuyako, monga wanena Yehova.

52. Ndipo panali pamene anamva mauwo mnyamata wa Abrahamu, anamgwadira Yehova pansi,

53. Ndipo mnyamatayo anaturutsa zokometsera zasiliva ndi zokometsera zagolidi, ndi zobvala, nampatsa Rebeka: ndipo anapatsa za mtengo wapatari kwa mlongo wace ndi amace.

54. Ndipo anadya namwa iye ndi anthu amene anali pamodzi naye, nagonapo usiku: ndipo anauka m'mamawa, ndipo iye anati, Mundilole ine ndinke kwa mbuyanga.

55. Ndipo mlongo wace ndi amace anati, Namwali akhale ndi ife masiku akuwerengeka, afikire khumi; patsogolo pace iye adzamuka.

56. Ndipo iye anati kwa iwo, Musandicedwetse ine, pakuti Yehova wandiyendetsa bwino m'njira yanga: mundilole ine ndinke kwa mbuyanga.

57. Ndipo anati iwo, Tidzamuitana namwaliyo, tidzamfunsa pakamwa pace.

58. Ndipo anamuitana Rebeka nati kwa iye, Kodi udzanka pamodzi ndi munthuyo? Ndipo anati, Ndidzanka.

59. Ndipo anamlola Rebeka mlongo wao ndi mlezi wace, amuke pamodzi ndi mnyamata wace wa Abrahamu, ndi anthu ace.

60. Ndipo anamdalitsa Rebeka, nati kwa iye, Mlongo wathu ndiwe, iwe ukhale amai wa anthu zikwizikwi, mbeu zako zigonjetse cipata ca iwo akudana nao.

Werengani mutu wathunthu Genesis 24