Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 22:9-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo anafika kumalo komwe Mulungu anamuuza iye; ndipo Abrahamu anamanga guwa la nsembe nakonza nkhuni, namanga Isake mwana wace, namuika iye pa guwa la nsembe pamwamba pa nkhuni.

10. Ndipo Abrahamu anatambasula dzanja lace, natenga mpeni kuti amuphe mwana wace.

11. Koma mthenga wa Yehova anamuitana iye ndi mau odzera kumwamba, nati, Abrahamu, Abrahamu; ndi iye anati, Ndine pano.

12. Ndipo mthenga anati, Usaike dzanja lako pa mwana, usamcitire iye kanthu; cifukwa tsopano ndidziwa kuti iwe umuopa Mulungu, pakuti sunandikanize ine mwana wako, mwana wako wayekha.

Werengani mutu wathunthu Genesis 22